Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:14-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Popeza analaka-lakatu kucidikhako,Nayesa Mulungu m'cipululu.

15. Ndipo anawapatsa copempha iwo;Koma anaondetsa mitima yao.

16. Ndipo kumisasa anacita nao nsanje MoseNdi Aroni woyerayo wa Yehova.

17. Dziko lidayasama nilidameza Datani,Ndipo linafotsera gulu la Abiramu.

18. Ndipo m'gulu mwao mudayaka moto;Lawi lace lidapsereza oipawo.

19. Anapanga mwana wa ng'ombe ku Horebu,Nagwadira fano loyenga.

20. M'mwemo anasintha ulemerero waoNdi fanizo la ng'ombe Yakudya msipu.

21. Anaiwala Mulungu mpulumutsi wao,Amene anacita zazikulu m'Aigupto;

22. Zodabwiza m'dziko la Hamu,Zoopsa ku Nyanja Yofiira.

23. Potero Iye adati awaononge,Pakadapanda Mose wosankhika wace, kuima pamaso pace pagamukapo,Kubweza ukali wace ungawaononge,

24. Anapeputsanso dziko lofunika,Osabvomereza mau ace;

25. Koma anadandaula m'mahema mwao,Osamvera mau a Yehova.

26. Potero anawasamulira dzanja lace,Kuti awagwetse m'cipululu:

27. Kugwetsanso mbeu zao mwa amitundu,Ndi kuwabalalitsa m'maiko maiko.

28. Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori,Nadyanso nsembe za akufa.

29. Ndipo anamkwiyitsa nazo zocita zao;Kotero kuti mliri unawagwera.

30. Pamenepo panauka Pinehasi, nacita cilango:Ndi mliriwo unaletseka.

31. Ndipo adamuyesa iye wacilungamo,Ku mibadwo mibadwo ku nthawi zonse.

32. Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba,Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa:

33. Pakuti anawawitsa mzimu wace,Ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106