Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:10-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo anawapulumutsa m'dzanja la iye amene anawada,Nawaombola ku dzanja la mdani.

11. Ndipo madziwo anamiza owasautsa;Sanatsala mmodzi yense.

12. Pamenepo anabvomereza mau ace;Anayimbira comlemekeza.

13. Koma anaiwala nchito zace msanga;Sanalindira uphungu wace:

14. Popeza analaka-lakatu kucidikhako,Nayesa Mulungu m'cipululu.

15. Ndipo anawapatsa copempha iwo;Koma anaondetsa mitima yao.

16. Ndipo kumisasa anacita nao nsanje MoseNdi Aroni woyerayo wa Yehova.

17. Dziko lidayasama nilidameza Datani,Ndipo linafotsera gulu la Abiramu.

18. Ndipo m'gulu mwao mudayaka moto;Lawi lace lidapsereza oipawo.

19. Anapanga mwana wa ng'ombe ku Horebu,Nagwadira fano loyenga.

20. M'mwemo anasintha ulemerero waoNdi fanizo la ng'ombe Yakudya msipu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106