Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:1-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya.Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino:Pakuti cifundo cace ncosatha.

2. Adzafotokoza ndani nchito zamphamvu za Yehova,Adzamveketsa ndani cilemekezo cace conse?

3. Odala iwo amene asunga ciweruzo,Iye amene acita cilungamo nthawi zonse.

4. Mundikumbukile, Yehova, monga momwe mubvomerezana ndi anthu anu;Mundionetsa cipulumutso canu:

5. Kuti ndione cokomaco ca osankhika anu,Kuti ndikondwere naco cikondwerero ca anthu anu,Kuti ndidzitamandire pamodzi ndi colowa canu.

6. Talakwa pamodzi ndi makolo athu;Tacita mphulupulu, tacita coipa.

7. Makolo athu sanadziwitsa zodabwiza zanu m'Aigupto;Sanakumbukila zacifundo zanu zaunyinji;Koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.

8. Koma anawapulumutsa cifukwa ca dzina lace,Kuti adziwitse cimphamvu cace.

9. Ndipo anadzudzula Nyanja Yofiira, niiphwa:Potero anawayendetsa mozama ngati m'cipululu.

10. Ndipo anawapulumutsa m'dzanja la iye amene anawada,Nawaombola ku dzanja la mdani.

11. Ndipo madziwo anamiza owasautsa;Sanatsala mmodzi yense.

12. Pamenepo anabvomereza mau ace;Anayimbira comlemekeza.

13. Koma anaiwala nchito zace msanga;Sanalindira uphungu wace:

14. Popeza analaka-lakatu kucidikhako,Nayesa Mulungu m'cipululu.

15. Ndipo anawapatsa copempha iwo;Koma anaondetsa mitima yao.

16. Ndipo kumisasa anacita nao nsanje MoseNdi Aroni woyerayo wa Yehova.

17. Dziko lidayasama nilidameza Datani,Ndipo linafotsera gulu la Abiramu.

18. Ndipo m'gulu mwao mudayaka moto;Lawi lace lidapsereza oipawo.

19. Anapanga mwana wa ng'ombe ku Horebu,Nagwadira fano loyenga.

20. M'mwemo anasintha ulemerero waoNdi fanizo la ng'ombe Yakudya msipu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106