Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:9-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

10. Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.

11. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

12. Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

13. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

14. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

15. Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.

16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.

17. Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:

18. Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;

19. Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.

20. Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.

21. Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse:

22. Amange nduna zace iye mwini,Alangize akulu ace adziwe nzeru.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105