Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

7. Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi.

8. Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

10. Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.

11. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105