Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:5-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita;Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;

6. Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

7. Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi.

8. Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

10. Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.

11. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

12. Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

13. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

14. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

15. Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.

16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105