40. Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.
41. Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.
42. Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.
43. Potero anaturutsa anthu ace ndi kusekerera,Osankhika ace ndi kupfuula mokondwera.
44. Ndipo anawapatsa maiko a amitundu;Iwo ndipo analanda zipatso za nchito ya anthu:
45. Kuti asamalire malemba ace,Nasunge malamulo ace.Haleluya.