Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:29-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Anasanduliza madzi ao akhale mwazi,Naphanso nsomba zao.

30. Dziko lao linacuruka acule,M'zipinda zomwe za mafumu ao.

31. Ananena, ndipo inadza mitambo ya nchenche,Ndi nsabwe kufikira m'malire ao onse.

32. Anawapatsa mvula yamatalala,Lawi la moto m'dziko lao.

33. Ndipo anapanda mipesa yao, ndi mikuyu yao;Natyola mitengo kufikira m'malire ao onse.

34. Ananena, ndipo linadza dzombeNdi mphuci, ndizo zosawerengeka,

35. Ndipo zinadya zitsamba zonse za m'dziko mwao,Zinadyanso zipatso za m'nthaka mwao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105