16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.
17. Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:
18. Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;
19. Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.
20. Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.
21. Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse:
22. Amange nduna zace iye mwini,Alangize akulu ace adziwe nzeru.
23. Pamenepo Israyeli analowa m'Aigupto;Ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.