Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.

16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.

17. Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:

18. Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;

19. Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.

20. Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.

21. Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse:

22. Amange nduna zace iye mwini,Alangize akulu ace adziwe nzeru.

23. Pamenepo Israyeli analowa m'Aigupto;Ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.

24. Ndipo anacurukitsatu mtundu wa anthu ace,Nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa.

25. Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ace,Kuti acite monyenga ndi atumiki ace.

26. Anatuma Mose mtumiki wace, Ndi Aroni amene adamsankha.

27. Anaika pakati pao zizindikilo zace,Ndi zodabwiza m'dziko la Hamu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105