Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

14. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

15. Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.

16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.

17. Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:

18. Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;

19. Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.

20. Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105