Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 105:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita Iye.

2. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

3. Mudzitamandire ndi dzina lace loyera:Mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.

4. Funani Yehova, ndi mphamvu yace;Funsirani nkhope yace nthawi zonse.

5. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita;Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;

6. Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

7. Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi.

8. Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

10. Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.

11. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

12. Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 105