Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 102:8-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Adani anga anditonza tsiku lonse;Akundiyarukirawo alumbirira ine.

9. Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,

10. Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.

12. Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse;Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.

13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.

14. Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yace,Nacitira cifundo pfumbi lace.

15. Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;

16. Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,Anaoneka m'ulemerero wace;

17. Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,Osapepula pemphero lao.

18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,

21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 102