Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 102:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota;Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5. Cifukwa ca liu la kubuula kwangaMnofu wanga umamatika ku mafupa anga.

6. Ndikunga bvuwo m'cipululu;Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7. Ndidikira, ndikhala ngati mbawaIri yokha pamwamba pa tsindwi.

8. Adani anga anditonza tsiku lonse;Akundiyarukirawo alumbirira ine.

9. Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,

10. Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 102