Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 102:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

22. Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.

24. Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.

25. Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 102