Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 102:2-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;Mundichereze khutu lanu;Tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga,

3. Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,Ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4. Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota;Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5. Cifukwa ca liu la kubuula kwangaMnofu wanga umamatika ku mafupa anga.

6. Ndikunga bvuwo m'cipululu;Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7. Ndidikira, ndikhala ngati mbawaIri yokha pamwamba pa tsindwi.

8. Adani anga anditonza tsiku lonse;Akundiyarukirawo alumbirira ine.

9. Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,

10. Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.

12. Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse;Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.

13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 102