Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 102:18-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,

21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

22. Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.

24. Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.

25. Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.

26. Zidzatha izi, koma Inu mukhala:Inde, zidzatha zonse ngati cabvala;Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:

27. Koma Inu ndinu yemweyo,Ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28. Ana a atumiki anu adzakhalitsa,Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 102