11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.
12. Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse;Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.
13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.
14. Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yace,Nacitira cifundo pfumbi lace.
15. Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;
16. Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,Anaoneka m'ulemerero wace;
17. Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,Osapepula pemphero lao.
18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.
19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;
20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,