Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 10:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Alalira monga mkango m'ngaka mwace;Alalira kugwira wozunzika:Agwira wozunzika, pakumkola m'ukonde mwace.

10. Aunthama, nawerama,Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.

11. Anena m'mtima mwace, Mulungu waiwala;Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,

12. Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;Musaiwale ozunzika.

13. Woipa anyozeranii Mulungu,Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?

14. Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu;Waumphawi adzipereka kwa Inu;Wamasiye mumakhala mthandizi wace.

15. Thyolani mkono wa woipa;Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.

16. Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;Aonongeka amitundu m'dziko lace.

17. Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika:Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:

18. Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 10