Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 10:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace,Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

4. Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.

5. Mayendedwe ace alimbika nthawi zonse;Maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;Adani ace onse awanyodola.

6. Ati mumtima mwace, Sindidzagwedezeka ine;Ku mibadwo mibadwo osagwa m'tsoka ine.

7. M'kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera;Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 10