Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 10:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu;Waumphawi adzipereka kwa Inu;Wamasiye mumakhala mthandizi wace.

15. Thyolani mkono wa woipa;Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.

16. Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;Aonongeka amitundu m'dziko lace.

17. Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika:Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:

18. Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 10