Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 1:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;Wakupatsa cipatso cace pa nyengo yace,Tsamba lace lomwe losafota;Ndipo zonse azicita apindula nazo.

4. Oipa satero ai;Koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

5. Cifukwa cace oipa sadzaimirira pa mlanduwo,Kapena ocimwa mu msonkhano wa olungama.

6. Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;Koma mayendedwe a oipa adzatayika.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 1