3. Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;Wakupatsa cipatso cace pa nyengo yace,Tsamba lace lomwe losafota;Ndipo zonse azicita apindula nazo.
4. Oipa satero ai;Koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.
5. Cifukwa cace oipa sadzaimirira pa mlanduwo,Kapena ocimwa mu msonkhano wa olungama.
6. Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;Koma mayendedwe a oipa adzatayika.