Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:48-63 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

48. M'diso mwanga mutsikamitsinje ya madzi cifukwa ca mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga woonongedwa,

49. Diso langa lingotsanulira osaleka, osapumula,

50. Kufikira Yehova adzazolika kumwamba ndi kuona;

51. Diso langa limvetsa moyo wanga zowawa cifukwa ca ana akazi onse a m'mudzi mwanga.

52. Ondida opanda cifukwa anandiinga ngati mbalame;

53. Anaononga moyo wanga m'dzenje, naponya mwala pamwambapaine;

54. Madzi anayenda pamwamba pa mutu panga, ndinati, dalikhidwa.

55. Ndinaitana dzina lanu, Yehova, ndiri m'dzenje lapansi;

56. Munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi popfuulaine.

57. Munayandikira tsiku la kukuitanani ine; munati, Usaope.

58. Ambuye munanenera moyo wanga mirandu yace; munaombola moyo wanga.

59. Yehova, mwaona coipa anandicitiraco, mundiweruzire;

60. Mwaona kubwezera kwao konse ndi zopangira zao zonse za pa ine.

61. Mwamva citonzo cao, Yehova, ndi zopangira zao zonse za pa ine,

62. Milomo ya akutsutsana nane ndi zolingalira zao za pa ine tsiku lonse.

63. Taonani kukhala ndi kunyamuka kwao; ndine nyimbo yao.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3