Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:39-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Kodi munthu wamoyo adandauliranji pokhala m'zocimwa zace?

40. Tisanthule ntiyese njira zathu ntibwerenso kwa Yehova.

41. Titukulire mitima yathu ndi, manja athu omwe kwa Mulungu ali kumwamba.

42. Ife tilakwa ndi kupikisana nanu, ndipo Inu simunatikhululukira.

43. Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola, mwatipha osacitira cisoni.

44. Mwadzikuta ndi mtambo kuti pemphero lathu lisapyolemo.

45. Mwatiika pakati pa amitundu ngati zinyalala ndi za kudzala.

46. Adani athu onse anatiyasamira,

47. Mantha ndi dzenje zitifikira, ndiphokose ndi cionongeko.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3