Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:37-56 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndani anganene, conena cace ndi kucitikadi, ngati Ambuye salamulira?

38. Kodi m'kamwa mwa Wam'mwambamwamba simuturuka zobvuta ndi zabwino?

39. Kodi munthu wamoyo adandauliranji pokhala m'zocimwa zace?

40. Tisanthule ntiyese njira zathu ntibwerenso kwa Yehova.

41. Titukulire mitima yathu ndi, manja athu omwe kwa Mulungu ali kumwamba.

42. Ife tilakwa ndi kupikisana nanu, ndipo Inu simunatikhululukira.

43. Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola, mwatipha osacitira cisoni.

44. Mwadzikuta ndi mtambo kuti pemphero lathu lisapyolemo.

45. Mwatiika pakati pa amitundu ngati zinyalala ndi za kudzala.

46. Adani athu onse anatiyasamira,

47. Mantha ndi dzenje zitifikira, ndiphokose ndi cionongeko.

48. M'diso mwanga mutsikamitsinje ya madzi cifukwa ca mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga woonongedwa,

49. Diso langa lingotsanulira osaleka, osapumula,

50. Kufikira Yehova adzazolika kumwamba ndi kuona;

51. Diso langa limvetsa moyo wanga zowawa cifukwa ca ana akazi onse a m'mudzi mwanga.

52. Ondida opanda cifukwa anandiinga ngati mbalame;

53. Anaononga moyo wanga m'dzenje, naponya mwala pamwambapaine;

54. Madzi anayenda pamwamba pa mutu panga, ndinati, dalikhidwa.

55. Ndinaitana dzina lanu, Yehova, ndiri m'dzenje lapansi;

56. Munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi popfuulaine.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3