Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:26-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Nkokoma kuti munthu ayembekeze ndi kulindirira modekha cipulumutso ca Yehova.

27. Nkokoma kuti munthu asenze gori ali wamng'ono.

28. Akhale pa yekha, natonthole, pakuti Mulungu wamsenzetsa ilo.

29. Aike kamwa lace m'pfumbi; kapena ciripo ciyembekezo.

30. Atembenuzire wompanda tsaya lace, adzazidwe ndi citonzo.

31. Pakuti Yehova sadzataya kufikira nthawi zonse,

32. Angakhale aliritsa, koma adzacitira cisoni monga mwa kucuruka kwa zifundo zace.

33. Pakuti samasautsa dala, ngakhale kumvetsa ana a anthu cisoni.

34. Kupondereza andende onse a m'dziko,

35. Kupambutsa ciweruzo ca munthu pamaso pa Wam'mwambamwamba,

36. Kukhotetsa mlandu wa munthu, zonsezi Ambuye sazikonda.

37. Ndani anganene, conena cace ndi kucitikadi, ngati Ambuye salamulira?

38. Kodi m'kamwa mwa Wam'mwambamwamba simuturuka zobvuta ndi zabwino?

Werengani mutu wathunthu Maliro 3