Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:25-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Yehova akhalira wabwino omlindirira, ndi moyo womfunafuna.

26. Nkokoma kuti munthu ayembekeze ndi kulindirira modekha cipulumutso ca Yehova.

27. Nkokoma kuti munthu asenze gori ali wamng'ono.

28. Akhale pa yekha, natonthole, pakuti Mulungu wamsenzetsa ilo.

29. Aike kamwa lace m'pfumbi; kapena ciripo ciyembekezo.

30. Atembenuzire wompanda tsaya lace, adzazidwe ndi citonzo.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3