Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Kumbukirani msauko Wanga ndi kusocera kwanga, ndizo civumulo ndi ndulu.

20. Moyo wanga uzikumbukirabe nuwerama mwa ine,

21. Ndiri naco ciyembekezo popeza ndilingalira ici ndiyembekeza kanthu.

22. Cifukwa cakusathedwa ife ndico cifundo ca Yehova, pakuti cisoni cace sicileka;

23. Cioneka catsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.

24. Moyo wanga uti, Gawo langa ndiye Yehova; cifukwa cace ndidzakhulupirira.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3