Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 3:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Watyolanso mano anga ndi tinsangalabwi, wandikuta ndi phulusa.

17. Watarikitsanso moyo wanga ndi mtendere; ndinaiwala zabwino.

18. Ndipo ndinati, Mphamvu yanga yatha, osayembekezanso kanthu kwa Yehova.

19. Kumbukirani msauko Wanga ndi kusocera kwanga, ndizo civumulo ndi ndulu.

20. Moyo wanga uzikumbukirabe nuwerama mwa ine,

21. Ndiri naco ciyembekezo popeza ndilingalira ici ndiyembekeza kanthu.

Werengani mutu wathunthu Maliro 3