Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 3:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mau anu andilimbira, ati Yehova. Koma inu mukuti, Tanena motsutsana nanu ndi ciani?

14. Mwanena, Kutumikira Mulungu nkwa cabe; ndipo tapindulanji ndi kusunga udikiro wace, ndi kuyenda obvala zamaliro pamaso pa Yehova wa makamu?

15. Ndipo tsopano tiwacha odzikuza odala, inde iwo ocita zoipa amangidwa ngati nyumba; inde, ayesa Mulungu, napulumuka.

16. Pamenepo iwo akuopa Yehova analankhulana wina ndi mnzace; ndipo Yehova anawachera khutu namva, ndi buku la cikumbutso linalembedwa pamaso pace, la kwa iwo akuopa Yehova, nakumbukila dzina lace.

17. Ndipo adzakhala anga anga, ati Yehova wa makamu, tsiku ndidzaikalo, ndipo ndidzawaleka monga munthu aleka mwana wace womtumikira.

18. Pamenepo mudzabwera ndi kuzindikira pakati pa wolungama ndi woipa, pakati pa iye wotumikira Mulungu ndi iye wosamtumikira.

Werengani mutu wathunthu Malaki 3