Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 2:6-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Cilamulo ca zoona cinali m'kamwa mwace, ndi cosalungama sicinapezeka m'milomo mwace; anayenda nane mumtendere ndi moongoka, nabweza ambiri aleke mphulupulu,

7. Pakuti milomo ya wansembe iyenera kusunga cidziwitso, ndi anthu ayenera kufunafuna cilamulo pakamwa pace; pakuti iye ndiye mthenga wa Yehova wa makamu.

8. Koma inu mwapambuka m'njira; mwakhumudwitsa ambiri m'cilamulo; mwaipsa cipangano ca Levi, ati Yehova wa makamu.

9. Cifukwa cace Inenso ndakuikani onyozeka ndi ocepseka kwa anthu onse, popeza simunasunga njira zanga, koma munaweruza mwankhope pocita cilamulo.

10. Kodi sitiri naye Atate mmodzi ife tonse? sanatilenga kodi Mulungu mmodzi? Ticita monyengezana yense ndi mnzace cifukwa ninji, ndi kuipsa cipangano ca makolo athu?

11. Yuda wacha monyenga, ndi m'Israyeli ndi m'Yerusalemu mwacitika conyansa; pakuti Yuda waipsa cipatuliko ca Yehova cimene acikonda, nakwatira mwana wamkazi wa mlungu wacilendo.

12. Yehova adzalikha munthu wakucita ici, wogalamutsa ndi wobvomereza m'tnahema a Yakobo, ndi iye wopereka copereka kwa Yehova wa makamu.

13. Ndi ici mubwereza kucicita: mukuta guwa la nsembe la Yehova ndi misozi, ndi kulira, ndi kuusa moyo; momwemo Iye sasamaliranso copereka, kapena kulandira mokondwera m'dzanja lanu.

14. Koma mukuti, Cifukwa ninji? Cifukwa kuti Yehova anali mboni pakati pa iwe ndi mkazi wa ubwana wako, amene unamcitira cosakhulupirika, cinkana iye ndiye mnzako, mkazi wa pangano lako.

15. Ndipo sanatero kodi wina womtsalira mzimu? Ndipo winayo anatero bwanji? Anatero pofuna mbeu ya Mulungu. Koma sungani mzimu wanu; ndipo asamcitire monyenga mkazi wa ubwana wace ndi mmodziyense.

Werengani mutu wathunthu Malaki 2