Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 7:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo cilamulo ca nsembe yoparamula ndi ici: ndiyo yopatulikitsa.

2. Pamalo pophera nsembe yopsereza ndipo aziphera nsembe yoparamula; nawaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.

3. Ndipo acotseko, nabwere nao mafuta ace onse; mcira wamafuta, ndi mafuta akukuta matumbo,

4. ndi imso ziwiri, ndi mafuta a pamenepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso;

5. ndipo wansembe atenthe izi pa guwa la nsembe, nsembe yamoto ya kwa Yehova; ndiyo nsembe yoparamula.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 7