Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 4:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo aturutse ng'ombeyo kunja kwa cigono, ndi kuitentha monga anatenthera ng'ombe yoyamba ija; ndiyo nsembe yaucimo ya kwa msonkhano.

22. Akacimwa mkuru, osati dala, pa cina ca zinthu ziti zonse aziletsa Yehova Mulungu wace, naparamula;

23. akamdziwitsa kucimwa kwace adacimwako, azidza naco copereka cace, ndico tonde wopanda cirema;

24. naike dzanja lace pamutu pa mbuziyo, naiphe pamalo pophera nsembe yopsereza pamaso pa Yehova; ndiyo nsembe yaucimo.

25. Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yaucimo ndi cala cace, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wace patsinde pa guwa la nsembe yopsereza.

26. Ndipo atenthe mafuta ace onse pa guwa la nsembe, monga mafuta a nsembe yoyamika; ndipo wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhululukidwa.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 4