Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 4:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Munthu akacimwa, osati dala, pa cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Mulungu, nakacitapo kanthu;

3. akalakwa wansembe wodzozedwa ndi kuparamulira anthu; pamenepo azibwera nayo kwa Yehova ng'ombe yamphongo, yopanda cirema, cifukwa ca kucimwa kwace adakucita, ikhale nsembe yaucimo.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 4