32. Ndipo limodzi la magawo khumi lonse la ng'ombe, kapena la nkhosa, kapena la mbuzi, ziri zonse zimapita pansi pa ndodo, limodzi la magawo khumi likhale lopatulikira Yehova.
33. Asafunse ngati yabwino kapena yoipa, kapena kuisintha; koma akaisinthatu, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika zonse ziwiri; asamaiombola.
34. Awa ndi malamulo, amene Yehova anauza Mose, awauze ana a Israyeli, m'phiri la Sinai.