Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 27:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Asamuombole munthu woperekedwa ciperekere kwa Mulungu; amuphe ndithu.

30. Limodzi mwa magawo khumi la zonse m'dziko, la mbeu zace za dziko, la zipatso za mtengo, ndilo la Yehova; likhale lopatulikira Yehova.

31. Koma munthu akaombolatu kanthu ka limodzi la magawo khumiwo aonjezeko limodzi la magawo asanu.

32. Ndipo limodzi la magawo khumi lonse la ng'ombe, kapena la nkhosa, kapena la mbuzi, ziri zonse zimapita pansi pa ndodo, limodzi la magawo khumi likhale lopatulikira Yehova.

33. Asafunse ngati yabwino kapena yoipa, kapena kuisintha; koma akaisinthatu, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika zonse ziwiri; asamaiombola.

34. Awa ndi malamulo, amene Yehova anauza Mose, awauze ana a Israyeli, m'phiri la Sinai.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 27