Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:50-55 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

50. Ndipo awerengere amene anamgulayo kuyambira caka adadzigulitsa kwa iye kufikira caka coliza lipenga; ndipo mtengo wace ukhale monga mwa kuwerenga kwa zaka; amuyesere monga masiku a munthu wolipidwa.

51. Zikamtsalira zaka zambiri, monga mwa izi abwezere ndarama zakumuombola zocokera ku ndalama zomgulazo.

52. Ndipo zikamtsalira zaka pang'ono kufikira caka coliza lipenga amwerengere; monga mwa zaka zace abwezere mtengo wace wakumuombola.

53. Akhale naye monga wolipidwa caka ndi caka; asamamlamulira momzunza pamaso pako,

54. Ndipo akapanda kumuombola motero, azituruka caka coliza lipenga, iye ndi ana ace omwe.

55. Pakuti ana a Israyeli ndi atumiki anga; iwo ndiwo atumiki anga amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25