Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Musamasautsana, koma uope Mulungu wako; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

18. M'mwemo mucite malemba anga, ndi kusunga maweruzo anga, ndi kuwacita; ndipo mudzakhala m'dzikomo okhazikika.

19. Dziko lidzaperekanso zipatso zace, ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi k'ukhalamo okhazikika.

20. Ndipo mukadzati, Tidzadyanji caka cacisanu ndi ciwiri? taonani, sitidzabzala, sitidzakolola dzinthu;

21. pamenepo ndidzauza dalitso langa litsike pa inu caka cacisanu ndi cimodzi, ndipo cidzapatsa zipatso zofikira zaka zitatu.

22. Ndipo mubzale caka cacisanu ndi citatu, ndi kudya zipatso zasundwe; kufikira caka cacisanu ndi cinai, mpaka zitacha zipatso zace mudzadya zasundwe.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25