Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Muciyese caka ca makomi asanuco coliza lipenga, musamabzala, kapena kuceka zophuka zokha m'mwemo; kapenakuceka mphesa zace za mipesa yosadzombola.

12. Popeza ndico caka coliza lipenga; muciyese copatulika, mudye zipatso zace kunja kwa munda.

13. Caka coliza lipenga ici mubwerere nonse ku zace zace.

14. Ndipo ukagulitsa kanthu kwa mnansi wako, kapena kugula kanthu ka mnansi wako, musamasautsana;

15. monga mwa kuwerenga kwace kwa zaka, citapita coliza lipenga, uzigula kwa mnansi wako, ndi monga mwa kuwerenga kwa zaka za zipatso azigulitsa.

16. Monga mwa kucuruka kwa zaka zace uonjeze mtengo wace, ndi monga mwa kucepa kwa zaka zace ucepse mtengo wace; pakuti akugulitsa powerenga masiku ace.

17. Musamasautsana, koma uope Mulungu wako; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

18. M'mwemo mucite malemba anga, ndi kusunga maweruzo anga, ndi kuwacita; ndipo mudzakhala m'dzikomo okhazikika.

19. Dziko lidzaperekanso zipatso zace, ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi k'ukhalamo okhazikika.

20. Ndipo mukadzati, Tidzadyanji caka cacisanu ndi ciwiri? taonani, sitidzabzala, sitidzakolola dzinthu;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25