Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 24:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. kutyola kulipa kutyola, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino; monga umo anacitira munthu cirema, momwemo amcitire iye.

21. Iye wakukantha nyama kuti ife, ambwezere yina; iye wakupha munthu, amuphe.

22. Ciweruzo canu cifanefane ndi mlendo ndi wobadwa m'dziko; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

23. Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, ndipo anaturutsa wotembererayo kunja kwa cigono, namponya miyala. Ndipo ana a Israyeli anacita monga Yehova adauza Mose.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 24