Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 23:29-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.

30. Ndi munthu ali yense wakugwira nchito iri yonse tsiku limenelo, ndidzaononga munthuyo pakati pa anthu a mtundu wace.

31. Musamagwira nchito iri yonse; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zoo nse.

32. Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzicepetse; tsiku lacisanu ndi cinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.

33. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

34. Nena ndi ana a Israyeli, kuti, Tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uno wacisanu ndi ciwiri pali madyerero a misasa a Yehova, masiku asanu ndi awiri.

35. Tsiku loyamba likhale msonkhano wopatulika, musamagwira nchito ya masiku ena.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 23