Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 23:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Nyengo zoikika za Yehova zimene muzilalikira zikhale masonkhano opatulika, ndizo nyengo zanga zoikika.

3. Masiku asanu ndi limodzi azigwira nchito; koma lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata lakupumula, msonkhano wopatulika; musamagwira nchito konse; ndilo sabata la Yehova m'nyumba zanu zonse.

4. Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, masonkhano opatulika, zimene muzilalikira pa nyengo zoikika zao.

5. Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, pali Paskha wa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 23