11. Asafike kuli mtembo; asadzidetse cifukwa ca atate wace, kapena mai wace.
12. Asaturuke m'malo opatulika, kapena kuipsa malo opatulika a Mulungu wace; popeza korona wa mafuta odzoza wa Mulungu wace ali pa iye; Ine ndine Yehova.
13. Ndipo adzitengere mkazi akali namwali.
14. Mkazi wamasiye, kapena womleka, kapena woipsidwa, wacigololo, oterewa asawatenge; koma azitenga namwali wa anthu a mtundu wace akhale mkazi wace.