Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 21:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Asafike kuli mtembo; asadzidetse cifukwa ca atate wace, kapena mai wace.

12. Asaturuke m'malo opatulika, kapena kuipsa malo opatulika a Mulungu wace; popeza korona wa mafuta odzoza wa Mulungu wace ali pa iye; Ine ndine Yehova.

13. Ndipo adzitengere mkazi akali namwali.

14. Mkazi wamasiye, kapena womleka, kapena woipsidwa, wacigololo, oterewa asawatenge; koma azitenga namwali wa anthu a mtundu wace akhale mkazi wace.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 21