Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 20:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Munthu akagona naye mkazi wa atate wace, wabvula atate wace; awaphe ndithu onse awiri; mwazi wao ukhale pamtu pao.

12. Munthu akagona ndi mpongozi wace, awaphe onse awiri; acita cisokonezo; mwazi wao ukhale pamtu pao.

13. Munthu akagonana ndi mwamuna mnzace, monga amagonana ndi mkazi, acita conyansa onse awiri; awaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.

14. Munthu akatenga mkazi pamodzi ndi mai wace cocititsa manyazi ici; aziwatentha ndi moto, iye ndi iwowa; kuti pasakhale cocititsa manyazico pakati pa inu.

15. Mwamuna akagona ndi nyama amuphe ndithu; muiphenso nyamayi.

16. Mkazi akasendera kwa nyama iri yonse kugonana nayo, umuphe mkaziyo, ndi nyama yomwe; muwaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 20