1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2. Nena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, nuti nao, Muzikhala oyera; pakuti ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndine woyera.
3. Ali yense aopemai wace, ndi atate wace; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.