Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 18:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. (pakuti eni dziko okhalako, musanafike inu, anazicita zonyansa izi zonse, ndi dziko linadetsedwa)

28. lingakusanzeni inunso dzikoli, polidetsa inu, monga linasanza mtundu wa anthu wokhalako musanafike inu.

29. Pakuti ali yense akacita ciri conse ca zonyansa Izi, inde amene azicita idzasadzidwa pakati pa anthu a mtundu wao.

30. Potero muzisunga cilangizo canga, ndi kusacita ziri zonse za miyambo yonyansayi anaicita musanafike inu, ndi kusadzidetsa nayo: Ine ndine Yehova Mulungu-wako.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 18