Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 18:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Usagona naye mkazi wa mnansi wako, kudetsedwa naye limodzi.

21. Ndipo usamapereka a mbumba yako kuwapitiriza kumoto cifukwa ca Moleke, usamaipsa dzina la Mulungu wako: Ine ndine Yehova.

22. Usamagonana ndi mwamuna, monga amagonana ndi mkazi; conyansa ici.

23. Ndipo usamagonana ndi nyama iri yonse, kudetsedwa nayo; kapena mkazi asamaima panyama, kugonana nayo; cisokonezo coopsa ici.

24. Musamadzidetsa naco cimodzi ca izi; pakuti amitundu amene ndiwapitikitsa pamaso panu amadetsedwa nazo zonsezi;

25. dziko lomwe lidetsedwa; cifukwa cace ndililanga, ndi dzikoli lisanza okhala m'mwemo.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 18