Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 18:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.

11. Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.

12. Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.

13. Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.

14. Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 18