1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Ine ndine Yehova Molungu wanu.
3. Musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Aigupto muja munakhalamo; musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Kanani kumene ndipita nanuko, nimusamayenda m'malemba ao.
4. Muzicita maweruzo anga, ndi kusunga malemba anga, kumayenda m'mwemo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5. Inde, muzisunga malemba anga, ndi maweruzo anga; amenewo munthu akawacita, adzakhala nao ndi moyo; Ine ndine Yehova.
6. Asasendere mmodzi wa inu kwa mbale wacekumbvula; Ine ndine Yehova.
7. Usamabvula atate wako, ndi mai wako; ndiye mai wako, usamambvula.
8. Usamabvula mkazi wa atate wako; ndiye thupi la atate wako.
9. Usamabvula mlongo wako, mwana wamkazi wa atate wako, kapena mwana wamkazi wa mai wako, wobadwa kwanu, kapena wobadwa kwina.