Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 18:1-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Ine ndine Yehova Molungu wanu.

3. Musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Aigupto muja munakhalamo; musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Kanani kumene ndipita nanuko, nimusamayenda m'malemba ao.

4. Muzicita maweruzo anga, ndi kusunga malemba anga, kumayenda m'mwemo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

5. Inde, muzisunga malemba anga, ndi maweruzo anga; amenewo munthu akawacita, adzakhala nao ndi moyo; Ine ndine Yehova.

6. Asasendere mmodzi wa inu kwa mbale wacekumbvula; Ine ndine Yehova.

7. Usamabvula atate wako, ndi mai wako; ndiye mai wako, usamambvula.

8. Usamabvula mkazi wa atate wako; ndiye thupi la atate wako.

9. Usamabvula mlongo wako, mwana wamkazi wa atate wako, kapena mwana wamkazi wa mai wako, wobadwa kwanu, kapena wobadwa kwina.

10. Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.

11. Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.

12. Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.

13. Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.

14. Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.

15. Usamabvula mpongozi wako; ndiye mkazi wa mwana wamwamuna wako; usamambvula.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 18